FAM YAPEPESA KWA MFUMU YAKU LILONGWE
Bungwe loyendetsa mpira mu dziko lino la Football Association of Malawi latulutsa kalata yopepesa kwa mfumu ya mzinda wa Lilongwe, a Peter Banda, kamba kokanizidwa kukapereka nawo mphoto kwa osewera pamathero a chikho cha NBS Bank Charity Shield.
Izi zadza patangodutsa maola ochepa unduna wa achinyamata, chikhalidwe ndi masewero komanso mtsogoleri wa bungwe la ma khonsolo mdziko muno, a Isaac Jomo Osman, anauza FAM kuti ipepese.
Bungweli lati silinachite kukonza kuti lichitire chipongwe mfumuyi koma ena omwe amayendetsa zinthu pa bwalo pomwepo anaona kuti zinthu zina zisokonekera malingana ndi momwe anakonzera.
Iwo ati akufufuza momwe zinthu zonse zinayendera kuti apeze chenicheni chimene chinachitika pa mwambowu.
0995587166
0991769328
0882410060
Tipepese kuti panali kusintha kwa mmene gemu ya Mamelodi Sundowns vs Esperance ya Loweruka pa 18 April imene inathera 1-0 koma poyamba tinaika molakwika kuti inatherka 0-0. Kusinthaku kwasintha omwe ali ap top 3 kuchoka pa olosera 13 kufika pa 9. Pano tatumiza ndalama kwa olosera 9 omwe apambana.
Choncho tikupepesa kwa olosera 4 omwe anali pa top 3 poyamba koma pano achoka.
Login with Facebook to post predictions, updates & live scores