Login with Facebook to post predictions, updates & live scores
CAF YAKHULUPILIRA AMALAWI ATATU
Bungwe loyendetsa mpira mu Africa la Confederation of African Football (CAF) lapereka maudindo kwa a Malawi atatu pa mpikisano wa masukulu amu Africa omwe uyambe pa 21 May ku Zanzibar.
Atatuwa ndi mkulu woona za mipikisano ku bungwe la Football Association of Malawi, Gomegzani Zakazaka komanso oyimbira awiri, Faith Gondwe komanso Wyson Mustafa, ndipo akagwira ntchito ku mpikisanowu.
Iwo adalinso pa mpikisano wa COSAFA wopitira ku mpikisano wa Africa yonse ndipo akuyembekezeka kunyamuka lero kulowera ku Zanzibar komwe mpikisanowu ukathe pa 24 May 2024.
SAPOTA WA FOMO WAMENYEDWA PA CIVO
Wachiwiri wa wapampando wa komiti ya ochemelera a timu ya FOMO mchigawo chapakati, Peter Malata ali ku chipatala komwe akulandira thandizo atamenyedwa ndi anthu omwe akuganiziridwa kuti ndi masapota atimu ya Clerk Sporting club.
Malingana ndi mlembi wamkulu wa komiti ya masapota FOMO mchigawochi, Felix Gunya, wati anthuwa anafika pa bwalo la CIVO kuzachita za zikhulupiliro zawo pamapeto a zokonzekera za timu ya FOMO, ndipo pokanizidwa kulowa mu bwaloli anayamba kumenya wachitetezo wa FOMO pamodzi ndi wapampandoyi.
Iye wati mwamwayi, wachitetezo anapeza mpata othawa ndipo tsopano ali ku chipatala.
Matimu a Creck Sporting Club komanso FOMO akumane pa masewero awo mu TNM Supa ligi pa bwalo la Civo pa nkhondo yotolera mapointsi.
Source: FOMO FC
"TIKUKAPAMBANA MWA NJIRA ILIYONSE" - BUNYA
Mphunzitsi watimu ya Dedza Dynamos, Andrew Bunya, wati timu yake ikhale ikupeza chipambano mwa njira iliyonse pomwe akhale akusewera pakhomo loweruka.
Iye amayankhula patsogolo pa masewero omwe asewere ndi Chitipa United pa bwalo la Dedza ndipo wati zokonzekera zawo zayenda bwino ndipo chatsala ndi kupeza chipambano basi.
"Zokonzekera zayenda bwino kwambiri ndipo anyamata akuoneka bwino kutengera ndi mmene akuthamangira komanso ku mbali ya ovulala nde tili okondwa ndi mmene tilili ndipo mwa njira iliyonse mawa tipeza chipambano." Anatero Bunya.
Iye anati akudalira osewera aliyense poti onse ali mu dongosolo lake ndipo malingana ndi mpikisano pakati pa anyamatawo akumasowa kuti ayambitsa ndani.
Timu ya Dedza ili pa nambala yachikhumi (10) pomwe yatolera mapointsi asanu ndi awiri (7) pa masewero asanu ndi amodzi (6) omwe yasewera.
"WE WILL FIGHT FOR A WIN" - MWANSA
Moyale Barracks head coach, Prichard Mwansa, says he expects a tough match as they face their fellow soldiers, Kamuzu Barracks but said they will play their normal game so they fight for a win.
He spoke this ahead of the match at the Aubrey Dimba Stadium in Mchinji on Saturday and said they have prepared well for the match.
"We are well prepared for this match, I know it's going to be tough because KB also plays well but we are fully determined and will fight to a win on Saturday." Said Mwansa.
He further said that the fact that they will play for their very first time at the Dimba Stadium will not affect them as they will approach the game as any other match.
The team is on position number 7 with 9 points having won twice, drawn three times and lost once in their opening 6 matches of the League.
"WE NEED TO TREAT HAMMERS WITH RESPECT" - PASUWA
FCB Nyasa Big Bullets head coach, Callisto Pasuwa, has also warned his charges against underrating Mzuzu City Hammers saying the team is on its best making them to sit second in the League this season
He said this ahead of their meeting on Saturday at the Kamuzu Stadium and said they need to treat Hammers with respect so that they win the match.
"And again as I always preach, it's our mind that we can make us will games. If we treat Mzuzu City Hammers as Hammers we can call it then we can end up losing points so we need to be positive on our approach and everything then we will say we have won the match."
"There's no small team and for that Mzuzu City Hammers to be second it means something else, this season they have been playing good football and also we need to treat them with respect so that we can come up with all points." Said Pasuwa.
Meanwhile, he said that Ernest Petro had returned to the team's squad whilst others who were
"TAKONZA NDI PA BENCH POMWE" - NGINDE
Mphunzitsi watimu ya Creck Sporting Club, Macdonald Nginde Mtetemera, wati timu yake tsopano yakonza mavuto awo onse omwe amakumana nawo mmasewero omwe akhala asakuchita bwino ndipo akukhulupilira kuti achita bwino loweruka.
Iye amayankhula patsogolo pa masewero omwe asewere ndi timu ya FOMO pa bwalo la Civo ndipo wati akonzeka kuti akapambanepo pa masewerowa.
"Takonza monse pagolo, kumbuyo, pakati komanso kutsogolo, angakhale pa bench ndi malo nde takonzekera ndithu kuti tikatenge chipambano, tikuyenda tsopano bwino chifukwa tsopano timuyi ikukonzeka bwinobwino." Anatero Mtetemera.
Iye wati yakwana nthawi tsopano kuti awapepese masapota atimuyi ndi chipambano ndipo tsopano mwa njira iliyonse Iwo apambana.
Timu ya Creck Sporting Club ili pa nambala 11 pomwe yapambana masewero awiri, kufanana mphamvu kamodzi ndi kugonjanso katatu ndipo ali ndi mapointsi asanu ndi awiri (7).
"SITIKUTULUKA MU LIGI IFE" - MUYOMBE
Mphunzitsi watimu ya Baka City, Davie Muyombe, watsutsa zoti palibe chiopsezo kuti timu yake ituluka mu ligi poti wati agwiritsa ntchito mwayi pa masewero awo apakhomo.
Iye amayankhula atatha masewero omwe agonja 4-1 ndi timu ya Mighty Waka Waka Tigers lachinayi ndipo wati timu yawo singatuluke mu ligi.
"Kutuluka ayi aah sitingatuluke, lero zinangotivuta poti osewera ena kunalibe koma tikadzakhala pakwathu sitingamachite chonchi ndipo tidzawina pakhomo." Anatero Muyombe.
Timu ya Baka City sinapambaneko masewero aliwonse mu ligiyi chilowereni pomwe yagonja kasanu ndi kufanana mphamvu kawiri ndipo ili ndi mapointsi awiri pa masewero asanu ndi awiri.
"TIKADALI NDI NTCHITO YOTI TIKONZE TIMUYI" - MPULULA
Mphunzitsi watimu ya Mighty Waka Waka Tigers, Leo Mpulula, wati ali ndi ntchito yaikulu yoti agwire kutimuyi kuti ikhale bwino pomwe akufunitsitsa kuti achite bwino mu ligi ya 2024.
Mpulula amayankhula atatha masewero omwe apambana 4-1 ndi timu ya Baka City lachinayi ndipo wati ngakhale apambana, zambiri zikuyenera kukonzedwa.
"Anali masewero abwino poti tapambana masewerowa komabe ntchito ilipo yoti tikonze kuti timuyi izisewera bwino komanso mipata yochuluka nde tayiphonya nde komabe tikonza." Anatero Mpulula.
Iye wati kugoletsa zigoli zinayi zikuonetsa kuti zomwe akuwaphunzitsa osewera ake zikugwira ntchito komabe zina azizidziwa mochedwerapo.
Timuyi yafika pa nambala yachisanu pomwe ali ndi mapointsi khumi ndi imodzi (11) pa masewero asanu ndi awiri (7).
Two charged over illegal sale of tickets
The Blantyre Resident Magistrate court have charged two individuals, Francis Danger and Samson White, after found guilty of selling tickets in the game involving Mighty Mukuru Wanderers and Karonga United last Saturday.
The two appeared before the court on the same day after being apprehended by the police after reports that they were selling tickets on the match day despite not being accredited to do the job.
They have been charged with an offence if being found with in possession of property suspected to be stolen, in contrary to section 329 as read with section 34 of the penal code.
Meanwhile, the super League of Malawi has reminded all stakeholders that it is punishable by law to be found with matchday tickets for the elite league matches without proper procedures and may led to criminal prosecution.
Danger, aged 24, hails from Konzere Village T/A Ngabu in Chikwawa district while Samson who is aged 35 comes from Machinga District T/A St
2-1
NO SERIOUS INJURIES IN NTOPWA'S ACCIDENT
No serious injury has been recorded as 6 Ntopwa Queens players have been treated as out patients after the team got involved in a car accident as they were travelling back from Lilongwe on Tuesday night.
This has been confirmed by the team's owner and head coach, Isaac Jomo Osman who said all those who got injured have been treated at Queen Elizabeth Central Hospital on Wednesday.
"I can confirm that there are no serious injuries on our girls. They just have minor injuries. Out of the 26 girls, six had minor and have been treated as out patients and they are now at home." Wrote Osman.
Meanwhile, he went on to thank Football Association of Malawi President, Fleetwood Haiya, National Women's Football Association Chairperson, Adelaide Migogo, FAM Chairperson for the competitions committee, Hon. Felistas Dossi, their Sponsor Kukoma and all other people for their assistance after the accident.
"Thanks to all the people for being with us throughout the night up to the time we arrived home." He added.
The team's bus was involved in an accident at Lizulu in Ntcheu after the driver tried to run from a convoy by State President, Dr Lazarus McCarthy Chakwera, and landed on an ox-cart on the side of the road.
The team was coming from Lilongwe where they were knocked out of the Goshen National Women's Football Championship after a 4-0 defeat over Ascent Academy on the same day.
0-1
Four awards of same kind
Tabitha Chawinga was yesterday awarded as the best player of the 2023/24 D1 Arkema season and also got a place in the team of the season in the League at Trophees UNFP.
This comes after having a stellar performance in the season which saw her netting 18 goals and providing 10 assists despite being her debut season.
Chawinga was awarded the same awards last week by D1 Arkema and these are of another kind. In the season, Chawinga also won two player of the month awards, missed one and also missed the goal of the month award.
Her contract ends after the season which ends on Friday as PSG play Olympic Lyonnais in the D1 Arkema playoffs Championship final and has already won the CoupΓ© de France with PSG.
In 2022/23 season, she won three awards that included the two when playing in Italy with Inter Milan.
3-0
2-0